Publicidade

Jeremias 20

14 Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa!

Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!

15 Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga

ndi uthenga woti:

"Kwabadwa mwana wamwamuna!"

16 Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene

Yehova anayiwononga mopanda chisoni.

Amve mfuwu mmawa,

phokoso la nkhondo masana.

17 Chifukwa sanandiphere mʼmimba,

kuti amayi anga asanduke manda anga,

mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.

18 Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni

kuti moyo wanga

ukhale wamanyazi wokhawokha?

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-22_10-02-25-