Publicidade

Jeremias 31

31 "Masiku akubwera," akutero Yehova,

"pamene ndidzachita pangano latsopano

ndi Aisraeli

ndiponso nyumba ya Yuda.

32 Silidzakhala ngati pangano

limene ndinachita ndi makolo awo

pamene ndinawagwira padzanja

nʼkuwatulutsa ku Igupto;

chifukwa anaphwanya pangano langa,

ngakhale ndinali mwamuna wawo,"

akutero Yehova.

33 "Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli

atapita masiku amenewo," akutero Yehova.

"Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo

ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo.

Ine ndidzakhala Mulungu wawo

ndipo iwo adzakhala anthu anga.

34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake,

kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, Mudziwe Yehova,

chifukwa onse adzandidziwa Ine,

kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,"

akutero Yehova.

"Ndidzawakhululukira zoyipa zawo

ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo."

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-