Publicidade

Zacarias 10

Yehova Adzasamalira Yuda

1 Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira;

ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula.

Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu,

ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.

2 Mafano amayankhula zachinyengo,

owombeza mawula amaona masomphenya abodza;

amafotokoza maloto onama,

amapereka chitonthozo chopandapake.

Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika

chifukwa chosowa mʼbusa.

3 "Ine ndawakwiyira kwambiri abusa,

ndipo ndidzalanga atsogoleri;

pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira

nkhosa zake, nyumba ya Yuda,

ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.

4 Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya,

mudzachokera chikhomo cha tenti,

mudzachokera uta wankhondo,

mudzachokera mtsogoleri aliyense.

5 Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo

zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo.

Chifukwa Yehova adzakhala nawo,

adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.

6 "Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda

ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe.

Ndidzawabwezeretsa

chifukwa ndawamvera chisoni.

Adzakhala ngati kuti

sindinawakane,

chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo

ndipo ndidzawayankha.

7 Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu

adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo.

Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala;

mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.

8 Ndidzaliza mluzu

ndi kuwasonkhanitsa pamodzi.

Ndithu ndawawombola;

adzachulukana ngati poyamba paja.

9 Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu,

koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira.

Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka,

ndipo adzabwerera.

10 Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto

ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya.

Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni,

mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.

11 Adzawoloka nyanja ya masautso;

nyanja yokokoma idzagonja

ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa.

Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha

ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.

12 Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova

ndipo adzayenda mʼdzina lake,"

akutero Yehova.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-