Ajuda ao próximo
Ajudar o próximo é mandamento de Deus e expressão prática da fé. A Bíblia ensina que a fé sem obras é morta — e que servir ao menor dos irmãos é servir a Cristo.
Nidali ni njala mdanipacha chakudya, ni nidali nilujho mdanipacha majhi ya kumwa, ni nidali mlendo mdanilandila mnyumba zanu. Nidalibe njhalu mdaniveka, nidali odwala mdanidwaza ni nidali mndende mdaniyendela.’ Pamenepo wandhu abwino siamuyanghe Mbuye, ‘Liti tidakuonani muli ninjala tidakupachani chakudya ni liti mudali ni lujho tidakupachani majhi ya kumwa? Liti tidakuonani mwali alendo niife kukulandilani kapina udalibe njhalu ni tidakupacha njhalu? Liti mumadwala kapina mwamangidwa mndende tidakuyendelani?’ Mfumu siwaayanghe, ‘Zene nikukambilani, umo mwamchitila mmojhi wa anyiyawa abale wanga yawo sajhikoza, mwanichitila ine!’"
Mundhu uyo wakupembha kandhu mpache. Uyo wafuna kukukongola usadammana."
Chimwecho dangalila lanu liwale pamaso pa wandhu kuti apenye vichito vanu vabwino ni kwaakweza Atate wanu akumwamba."
Apacheni wandhu wina vindhu, ni Mnungu siwakupacheni anyiimwe. Zenedi, simlandile mmanja mwanu chipimo chojhala ni kuchindilidwa bwino mbaka kumwazika, pakuti chichijha mwapimila wina, nianyiimwe simpimilidwe chimwecho ni Mnungu."
Gulu la wandhu lijha lidamfunjha, "Chipano ifunika tichite chiyani?" Yohana wadayangha, "Uyo wali ni njhalu ziwili wamgawile uyo walibe, ni uyo wali ni chakudya wamgawile uyo walibe."
Gulichani vyuma vanu ni mwaninghe ndalama wandhu wosauka ndalama zimenezo. Mujhikonjele matumba ya ndalama yosatha ni ikilani chuma kumwamba icho sichichepa, kumalo uko anghungu sakhoza kuba ni vidudu kuwananga. Ndande yake, yapo waikila chuma chako ndeyapo umoyo wako siukhalepo."
Lamulo langa nde ili, mkondane ngati ine umo nidakukondelani anyiimwe.
Palibe chikondi chachikulu kupunda kusiyana ni chikondi cha mundhu uyo wachocha umoyo wake ndande ya bwenji lake.
Siku zonjhe nachita njhito ngati chifani kwanu, kulangiza kuti tifunika kwatangatila osauka, uku nitikumbukila mawu ya Ambuye Yesu mwene yayo yakamba, ‘Ali ni mwawi anyiawo achocha kusiyana ni anyiiawo alandila.’"
Poolo yapo wadamaliza kukamba chimwechi wadagwada pamojhi ni anyiiwo wonjhe, ndiipo adampembha Mnungu. Wandhu wonjhe adalila ni kumvumbatila Poolo, ndiipo adamlaila. Icho chidaadandaulicha ni yajha mawu wadaakambila Poolo kuti samuonanjho. Ndiipo adampelekeza mbaka ku sitima.
Mwathangatile okhulupila Mnungu achanjanu ivo savifune, alandileni alendo kwa kukondwela.
Athangatileni wina
Ife yao takwima mchikhulupi ifunuka taathangatile anyiwajha afooka, kuti ayakhoze mavuto yao. Tisidajhikondelela tachinawene pe.
Mthangatilane anyiimwe kwa anyiimwe kwakuchita chimwecho simkwanilichwe thauko la Kilisito.
Uyo wakuba, siwadabanjho, nambho wayambe kuchita njhito yabwino kwa manja yake, dala wakhale ni chindhu cha kumthangatila osauka.
Kila mmojhi siwadajhipenya kupata kwake mwenepe, nambho wapenye kupata kwa mnjake.