1 Kuchokana ni yameneyo, ine Poolo uyo namangidwa ndande ya kumtumikila Kilisito Yesu ndande ya anyiimwe, wandhu asati Ayahudi nimpembha Mnungu. 2 Nijhiwa mwathovela kuti Mnungu kwa ubwino wake, wadanipacha njhito iyi yakukulalikilani anyiimwe Uthenga Wabwino. 3 Ine nidajhiwichidwa chindhu ichi chobisika kupitila chisisi, nane nachilemba chindhu ichi kwa mau yochepa, 4 namwe mkayasoma mau yanga simujhiwe umo nichijhiwila chisisi chimemenecho cha nghani ya Kilisito. 5 Chisisi chimenecho, siwadachijhiwichepo kwa wandhu akale, nambho chipano wajhiwicha chisisi chimenecho atumwi ni alosi yawo asanghidwa kwa kupitila Mzimu wa Mnungu. 6 Chisisi chimenecho ni kuti, kwa kupitila Uthenga Wabwino wandhu asati Ayahudi apata yajha Mnungu wadakamba kuti siwapache Ayahudi. Anyiiwo ni viwalo va thupi limojhi ni ogwilizana achijha wadakamba Mnungu kuti siwapache kupitila Yesu Kilisito.
7 Ine nachitidwa kukhala Mtumiki wa kulalikila Uthenga Wabwino kwa ubwino wa Mnungu uwo wanipacha kuchokana ni kukhoza kwake kwa kukulu. 8 Ine nili wamng'ono kulekana ni wandhu onjhe wa Mnungu, nambho wanipacha ine ubwino wake kuti nalalikile wandhu asati Ayahudi ubwino wa Kilisito uwo siufotokozeka, 9 kuika padanga kwa wandhu onjhe aone mpango uwo Mnungu uwo wabisika umo ukwanilichidwa. Mnungu uyo waumba vindhu vonjhe wadachibisa chisisi chimenecho kuyambila kale, 10 dala kwa kupitila gulu la wandhu amkhulupilila Kilisito, afumu ni alamuli akumwamba aijhiwe hekima ya Mnungu iyo ili ya mtundu wambili. 11 Mnungu wadachita chimwechi kuchokana ni dala lake la muyaya ilo wadachita kupitila Yesu Kilisito Ambuye wathu. 12 Chipano kwa kulunjana ni Kilisito ni kumkhulupilila, tipilila kumuwandikila Mnungu kwa kumkhulupilila. 13 Chimwecho simudafa mtima ndande ya mavuto yayo nipata ine ndande yanu, yameneyo yakuchitani mlemekezeke.
14 Chipano nimphembha Mnungu Tate kwa kumgwadila, 15 uyowali chiyambo cha voumbidwa vonjhe va kumwamba ni pajhiko. 16 Nimpembha Mnungu, wakupacheni ngati umo kuli kuchuluka kwa ulemelelo wake, wakupacheni mbhavu za mzimu wake, ni mbhavu mkati mwanu yoima nganganga, 17 dala Kilisito wakhale mkati mwanu kwa njila ya kumkhulupilila. Nimpembha Mnungu yonjhe yayo muyachita yachoke muchikondi cha zene, 18 dala anyiimwe pamojhi ni wandhu onjhe a Mnungu, mjhiwe umo Kilisito watikondela kupunda kwa chikondi icho chilibe mathelo, 19 ni mujhiwe chikondi cha Kilisito icho chipitilila umo ajhiwila wandhu wonjhe, mukhale wokwanila kupunda kwa Mnungu.
20 Iye uyo wakhoza kuchita vindhu vodabwicha kupunda kupitilila vijha tivipembha ni kuvighanizila. Kuchokana ni mbhavu zake izo zichita njhito mkati mwathu. 21 Watamandidwe, ulemelelo wake ukhale kwa gulu la wandhu wonjhe akhulupilila Kilisito ni kwa Kilisito Yesu ndhawi zonjhe, Muyaya ni muyaya! Ikhale chimwecho.