1 "Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,
bwerani madzi alipo;
ndipo inu amene mulibe ndalama
bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!
Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka
osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,
ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?
Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;
ndipo mudzisangalatse.
3 Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;
mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.
Ndidzachita nanu pangano losatha,
chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,
kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,
ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.
Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,
Woyerayo wa Israeli,
wakuvekani ulemerero."
6 Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.
Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.