Publicidade

Isaías 62

Dzina Latsopano la Ziyoni

1 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete,

chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete,

mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala,

ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.

2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo

ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako.

Adzakuyitanira dzina latsopano

limene adzakupatse ndi Yehova.

3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova,

ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.

4 Sadzakutchanso "Wosiyidwa,"

ndipo dziko lako silidzatchedwanso "Chipululu."

Koma dzina lako latsopano lidzakhala "Ndakondwera naye."

Ndipo dziko lako lidzatchedwa "Wokwatiwa."

Chifukwa Yehova akukondwera nawe,

ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.

5 Monga mnyamata amakwatira namwali,

momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira;

monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi,

chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.

6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda;

sadzakhala chete usana kapena usiku.

Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake

musapumule.

7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu

kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.

8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake.

Anati,

"Sindidzaperekanso tirigu wako

kuti akhale chakudya cha adani ako,

ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano

pakuti unamuvutikira.

9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi

ndi kutamanda Yehova,

ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo

mʼmabwalo a Nyumba yanga."

10 Tulukani, dutsani pa zipata!

Konzerani anthu njira.

Lambulani, lambulani msewu waukulu!

Chotsani miyala.

Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.

11 Yehova walengeza

ku dziko lonse lapansi kuti,

Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti,

"Taonani, chipulumutso chanu chikubwera;

Yehova akubwera ndi mphotho yake

akubwera nazo zokuyenerani."

12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika,

owomboledwa a Yehova;

ndipo adzakutchani "Okondwa a Yehova"

"Mzinda umene Yehova sanawusiye."

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-