10 Monga mvula ndi chisanu chowundana
zimatsika kuchokera kumwamba,
ndipo sizibwerera komweko
koma zimathirira dziko lapansi.
Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera
kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.
Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,
koma adzachita zonse zimene ndifuna,
ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.