9 Yehova anati, "Pita ndipo ukawawuze anthu awa:
" ‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa;
kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
10 Tsono anthu amenewa uwaphe mtima;
uwagonthetse makutu,
ndipo uwatseke mʼmaso.
Mwina angaone ndi maso awo,
angamve ndi makutu awo,
angamvetse ndi mitima yawo,
kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa."