3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,
nkhata ya maluwa yokongola
mʼmalo mwa phulusa,
ndiwapatse mafuta achikondwerero
mʼmalo mwa kulira.
Ndiwapatse chovala cha matamando
mʼmalo mwa mtima wopsinjika.
Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,
yoyidzala Yehova
kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.