Chiweruzo ndi Chiyembekezo
1 Yehova akuti,
"Kumwamba ndi mpando wanga waufumu
ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.
Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,
ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,
motero zonsezi ndi zanga?"
Akutero Yehova.
"Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:
amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,
ndipo amamvera mawu anga.