Publicidade

Isaías 66

Chiweruzo ndi Chiyembekezo

1 Yehova akuti,

"Kumwamba ndi mpando wanga waufumu

ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.

Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,

ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?

2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,

motero zonsezi ndi zanga?"

Akutero Yehova.

"Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:

amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,

ndipo amamvera mawu anga.

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-29_22-07-56-