Pular para o conteúdo
Publicidade

Isaías 9

6 Chifukwa mwana watibadwira,

mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife,

ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake.

Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti

Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu,

Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.

7 Ulamuliro ndi mtendere wake

zidzakhala zopanda malire.

Iye adzalamulira ufumu wake ali pa

mpando waufumu wa Davide,

ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza

mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo

kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya.

Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse

watsimikiza kuchita zimenezi.

Veja também