Pular para o conteúdo
Publicidade

Isaías 43

Yehova Yekha Mpulumutsi wa Israeli

1 Koma tsopano, Yehova

amene anakulenga, iwe Yakobo,

amene anakuwumba, iwe Israeli akuti,

"Usaope, pakuti ndakuwombola;

Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.

2 Pamene ukuwoloka nyanja,

ndidzakhala nawe;

ndipo pamene ukuwoloka mitsinje,

sidzakukokolola.

Pamene ukudutsa pa moto,

sudzapsa;

lawi la moto silidzakutentha.

3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako,

Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako.

Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe,

ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.

Veja também