Pular para o conteúdo
Publicidade

Isaías 53

3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu,

munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa,

ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona.

Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.

4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife;

ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu.

Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga,

kumukantha ndi kumusautsa.

5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu,

ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu;

iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere,

ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.

Veja também