5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu,
ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu;
iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere,
ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera,
aliyense mwa ife akungodziyendera;
ndipo Yehova wamusenzetsa
zoyipa zathu zonse.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa,
koma sanayankhule kanthu.
Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira,
kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta,
momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.