1 Kalata ino ichoka kwa ine Poolo uyo nili mtumwi osati kwa ulamulilo wa wandhu, ni osati kwa mbhavu za mundhu, nambho kwa mbhavu za Yesu Kilisito ni za Mnungu Tate uyo wadamuyukicha Yesu. 2 Ine ni anyaabale wonjhe yao ali pamojhi ni ine tikulonjelani anyiimwe mwamkhulupilila Yesu muli ku mujhi wa Galatiya. 3 Tikufunilani ubwino ni mtendele kuchokela kwa Tate wathu ni Ambuye watu Yesu Kilisito.
4 Kilisito wadajhichocha mwene ndande ya kuchocha machimo yathu ngati umo adafunila Amnungu kuti, wakhoze kutiombola mjhiko lino lajhala voipa. 5 Chipano ulemelelo ukhale kwa Mnungu muyaya ni muyaya! Amina.
6 Nizizwa kupunda ndande yandopitape ndhawi yochepa anyiimwe mwamsiya Mnungu uyo wadakutanani kwa ubwino wa Kilisito, anyiimwe mchata Uthenga wabwino wina uwo uoneka ngati Uthenga Wabwino. 7 Zenedi asati Uthenga Wabwino. Uzene ni kuti alipo wandhu yawo akusakalichani, wandhu yao afuna kuyapundula mayaluzo ya Kilisito. 8 Nambho ata ngati mmojhi wanu kapina mtumiki wa kumwamba wa Amnungu wakakulalikilani Uthenga wina uwo uoneneka ngati Uthenga Wabwino kusiyana ni ujha tidakulalikilani, walesedwe mundhu mmeneyo! 9 Ngati mujha tidakukambilani, ni saino nikambanjho, ngati mundhu waliyonjhe wakakulalikilani Uthenga wina kusiyana ni ujha mdalikidwa, walesedwe mundhu mmeneyo!
10 Chipano bwanji, nifuna kuvomelezedwa ni Amnungu kapina mundhu? Kapina nifuna kwakwadilicha wandhu? Ngati nidakafuna kumkondwelecha mundhu, sinidakakhala mtumiki wa Kilisito.
11 Achaabale wanga nifuna mjhiwe kuti, Uthenga Wabwino ujha nidakulakilani siuchokela kwa wandhu. 12 Ine sinidalandile kuchokela kwa wandhu, ni sinidayaluzidwe ni mundhu. Yesu Kilisito mwene nde uyo wanivunukulila.
13 Nijhiwa kuti mdathovela umo nimakhalila kale kuchatila chikalidwe cha Ayahudi yawo adamkhulupilila, niumo nidaavuticha wandhu adamkhulupilila Mnungu kwa mbhavu zambili ni kufuna kuyomwecha chikhulupi chawo. 14 Nane nidaakhoza anyamata anjanga ambili pa kuchatiza chikhalidwe chathu cha chiyahudi, nidajitahidi kupunda kugwila khalidwe lonjhe ilo nidalandila kuchokela kwa azee wathu.
15 Nambho idamkondwelecha Mnungu kunisanghula ine nikali osabadwe kuti nimtumikile. 16 Wadanivunukilila mwana wake umo wali, dala nikhoze kulalikila Uthenga wao wa Bwino kwa wandhu yawo opande Ayahudi. Ine sinidamfunjhe mundhu waliyonjhe, 17 sinidakwele kumujhi wa ku Yelusalemu kwa anyiwajha adali atumwi kabla ya ine, nambho nidapita kujhiko la Alabia ni kubwelanjho ku mujhi wa Damesiko. 18 Yapo vidapita vyaka vitatu nidapita ku mujhi wa Yelusalemu kupezana ni Petulo. Nidakhala kukhomo lake kwa masiku khumi ni yasano, 19 nambho sinidaone atumwi wina ingakhale Yakobo mpwake wa Ambuye Yesu. 20 Yaya nikulembelani, Amnungu ayajhiwa kuti sinikamba unami. 21 Yapo nidachoka ku mujhi wa Yelusalemu nidapita kumijhi ya Siliya ni Kilikia 22 Ndhawi imeneyo, ine sinimajhiwike ni ghulu la Akilisito kujha ku jhiko la Yudea. 23 Anyiiwo adandovelape nghani kuti, "Mundhu yujha mmayambo wamativuticha chipano walalikila chikhulupi chimchijha icho wafuna kuchiyomwecha." 24 Chimwecho adamtamanda Mnungu ndande yaine.