1 Ndiipo Siku lina lo Pumulila, Yesu wadalowanjho mnyumba yokomanilana Ayahudi, ni mujha mkati kudali ni mundhu uyo wali ni jhanja lovuwala. 2 Mmenemo, kudali Afalisayo akumojhi yawo amampenya amuone ngati samlamiche mundhu Siku lo Pumulila apate ndande ya kumgwila. 3 Yesu wadamkambila yujha mundhu wadali ni jhanja lovuwala, "Majha pano pakatikati." 4 Ndiipo wadaafunjha wandhu, "Bwanji, mathauko ya Musa yatifuna tichite chiyani pa Siku lo Pumulila? Bwanji, kuchita vabwino kapina kuchita voipa? Kuuwombola umoyo wa mundhu kapina kuupha?" Nambho anyiiwo adakhala chete. 5 Yesu wadaapenya wonjhe kwa mbhwayi, pamenepo wadaona chisoni mumtima mwake ndande ya kosakhulupilila kwawo. Ndiipo wadamkambila yujha mundhu, "Tambasula jhanja lako." Ni yujha wovuwala wadatambasula jhanja lake, ni kulama. 6 Chimwecho Afalisayo adatuluka kubwalo kwa nyumba yo komanilana Ayahudi, adakhala pamojhi ni agulu la wandhu yawo amamthangatila Helode, ni kukambilana umo siamphele Yesu.
7 Yesu wadachoka pamojhi ni oyaluzidwa wake, wadapita pafupi ni nyanja ya Galilaya, ni gulu la wandhu lidamchata. Wandhu ameneo adachokela ku Galilaya ni ku Yudea. 8 Yapo adavela yayo wadayachita Yesu, gulu lalikulu la wandhu lidamchata kuchokela ku Yudea ni Yelusalemu ni Iduneya ni vijhijhi ivo vidali kuchijya kwa mchinje Yolodani ni mijhi ya Tilo ni Sidoni. 9 Yesu wadaakambila oyaluzidwa wake amuikile bwato umojhi, kuti gulu la wandhu lisidamzengazenga, ndande wandhu adali ambili. 10 Wadaalamicha wandhu ambili, ni odwala ambili amatomzengazenga dala amgafye. 11 Wandhu yawo adali ni viwanda, yapo adamwona Yesu, adajhitaya panjhi pachogolo pake ni kukweza mvekelo, niakamba, "Iwe ni Mwana wa Mnungu!" 12 Nambho Yesu wadavikaniza vijha viwanda visadamkambila mundhu waliyonjhe kuusu nghani zake.
13 Yesu wadakwela kuphili, ni kwaatana anyiwajha wadaafuna, nawo adamchata. 14 Niiye wadaasangha khumi ni awili ni kwaatana atumwi, wadaakambila, "Nakusanghanai anyiimwe mukhale ni ine. Ndiipo sinikutumeni mukalalikile wandhu Uthenga Wabwino. 15 Namwe simukhale ni ulamulilo wotopola viwanda." 16 Anyiyawa nde wandhu khumi ni awili yawo wadaasangha, Simoni uyo Yesu wadamtana jhina lina Petulo, 17 ni Yakobo mphwake wa Yohana, wana a Zebadayo. Yesu wadaatana jhina la Boanelige, mateyake "Wana a mtungulu," 18 Andulea ni Filipo ni Batolomayo ni Matayo ni Tomaso ni Yakobo mwana wa Alifayo ni Tadayo ni Simoni uyo wamabulanila jhiko lake, 19 ni Yuda Isikaliyoti, yujha pambuyo wadamuukila Yesu.
20 Ndiipo Yesu wadabwela kukhomo. Gulu la wandhu lidaphezananjho mbaka Yesu ni ochatila wake sadakhoze kudya chakudya ndande wamatumikila wandhu. 21 Achabale wake yapo adavela nghani zimenezo adachoka ni kupita kumtenga, pakuti amakamba, "Wali ni msala."
22 Oyaluza athauko la Musa, yawo adachokela ku Yelusalemu, adakamba, "Wachogozedwa ni Belizabuli wamkulu wa viwanda, nde uyo wampacha mbhavu zotopola viwanda." 23 Yesu wadaatana ni kwaakambila kwa chifani, "Bwanji, Satana wakhoza kujhitopola mwenewake? 24 Ufumu uliwonjhe ukapatukana ni kubulana, ufumu umenewo siukhoza kulimba. 25 Ikakhala wandhu a nyumba imojhi apatukana achinawene magulumagulu yayo yachuchana, nyumba imeneyo siikhoza kulimba. 26 Ngati ufumu wa Satana wapatukana magulumagulu siukhoza kulimba, ni siugwe."
27 "Palibe mundhu wakhoza kuhundukila nyumba ya mundhu uyo wali ni mbhavu ni kumlanda chuma chake popande kummanga. Wakammanga ndeyapo siwakhoze kumlanda chuma chake."
28 "Zenedi nikukambilani, machimo yonjhe yayo achita wandhu, ni kukafula kwawo konjhe, Mnungu siwalekelele. 29 Nambho mundhu waliyonjhe uyo wamkafula Mzimu Woyela, kukafula kwake sikulekeleledwa muyaya. Ndande wachita machimo ya muyaya." 30 Yesu wadakamba chimwecho ndande anyiiwo amakamba, "Wali ni chiwanda."
31 Amake ni achabale wake Yesu adafika pamenepo, adaima kubwalo, adamtuma mundhu mkati kuti wakamtane Yesu. 32 Gulu la wandhu lidamzungulila Yesu. Nawo wandhu wajha adamzungulila adamkambila, "Amako ni achabale wako ali kubwalo, atokufuna iwe." 33 Yesu wadaafunjha, "Maye wanga ni achabale wanga ni achiyani?" 34 Pamenepo wadaapenya wandhu wajha adamzungulila ni kukamba, "Penyani, anyiyawa nde maye wanga ni achabale wanga auzene. 35 Mundhu waliwonjhe uyo wachita yayo wayafuna Mnungu, mmeneyo nde mkulu wanga ni mlongowanga ni maye wanga."