22 Achitadama kuti ali ni ekima, nambho ni asabwabwa. 23 Asiya kumlambila Mnungu wa muyaya, ni pambuyo pake, avilambila viboliboli vili chifani cha mundhu uyo wamwalila, chifani cha zinyama, mbalami ni vokwawa.
24 Ndande imeneyo, Mnungu wasiya achate khumbilo loipa la mitima yao, ni kuchitilana vindhu va njhoni achinawene kwa achinawene. 25 Aung’anamula uzene wa Mnungu ni kuuchita ukhale unami, achilemekeza ni kuchilambila choumbidwa ni Mnungu pambuyo pa kumlambila Mnungu mwene, uyo idafukika kulambilildwa muyaya! Ikhale chimwecho.
26 Chipano, Mnungu waasiya achate khumbilo loipa. Wachikazi ang’anamula matupi yawo, ni kutumila mosafunikile kwa kukhumbilana achinawene kwa achina wene. 27 Ni wachimuna chimwecho, asiya kukhumbilana wamnuna ni wamkazi, akhumbilana anyiiwo kwa anyiiwo. Wachimuna achitilana vindhu va njhoni, chimwecho saalangidwe kuchokana ni vichito vao voipa.