1 Chipano, achabale wanga, pakuti Mnungu ni walisungu kupunda, nikupembhani kwa mtima wanga wonjhe, mjhichoche mwachinawene kwa Amnungu mkhale ngati njhembe yo pyeleza iyo ili yamoyo, iyo ili ya Mnungu mwene ni yomkwadilicha Mnungu. Iyi nde njila yanu ya zene yakumlambila Mnungu. 2 Simudaganizila ngati wandhu ajhiko lino umo aganizila, nambho Mnungu siwakung'anamuleni maganizo yanu kwa kuganizila bwino. Pamenepo ndipo simkhoze kujhiwa icho wafuna Mnungu ni kujhiwa chindhu chili cha bwino, ilo limkwadilicha ni kuchita ngati umo ifunikila.
3 Kuchokana ni ubwino uwo wanipacha Mnungu, nikukambilani anyiimwe mwaonjhe, simdajhiona kuti anyiimwe ni abwino kusiyana ni umo mmafunika kukhala. Mjhipime mwachinawene umo muli kwa chipimo cha chikhulupi icho Mnungu wamgawila kila mmojhi, 4 Thupi ni limojhi ni lili ni viwalo vambili kila chiwalo chili ni jhito yake. 5 Ata ngati ife ni ambili, tili thupi limojhi kwa kulunjana ni Kilisito, ni kila mmojhi ni chilunjo cha mnjake 6 Chipano tili ni mbhaso zosiyana siyana kulingana ni ubwino uwo tapachidwa. Uyo wali ni mbhaso ya ulosi watumile kulingana ni chikhulupi chake. 7 Uyo wali ni mbhaso ya kutumikila ni watumikile. Uyo wali ni mbhaso yoyaluza wayaluze. 8 Uyo wali ni mbhaso yakwatila wina mtima wachite chimwecho. Uyo wamgawila mwina icho wali nacho wachite chimwecho kwa chikondi. Uyo waimilila waimile kwa mtima wake wonjhe, uyo wachita chindhu kwa lisungu wachite chimwecho kwa chikondi.
9 Kukondana kwanu ifunika sikudakhala ni ughunghuli walionjhe. Ipilani chindhu chalichonjhe choipa, chitani vindhu vabwino. 10 Kondanani anyiimwe kwa anyiimwe ni kwakonda okhulupilila achanjanu. Mumlemekeze uti kila mmojhi pakati panu. 11 Msidakhala alesi kuchita jhito ya Mnungu, mchite njhito imeneyo kwa mtima onjhe ni kumtumikila Mnungu. 12 Kukhulupilila kwanu kukuchiteni mkondwele ndhawi zonjhe, muembekeze mmavuto, ni kuphembela siku zonjhe. 13 Mwathangatile okhulupila Mnungu achanjanu ivo savifune, alandileni alendo kwa kukondwela.
14 Mwafunile ubwino yao akuchitilani voipa, mpembheni Mnungu wapache mwawi ni siwadaleswa. 15 Kondwelani pamojhi ni yawo akondwela, lilani pamojhi ni yao alila. 16 Mkhale kwakuvanichana bwino anyiimwe kwa anyiimwe. Simdajhidama nambho mjhichiche, mkhale ni mgwilizano apanjhi. Simdajhidama kuti muliojhiwa kupunda.
17 Simdabwelezela loipa kwa loipa, chitani vindhu ivo wandhu ajhiwa kuti vabwino. 18 Chitani umo ikhozekelana, mkhale kwa mtendele ni wandhu wonjhe. 19 Okondedwa wanga, simdabwelezela mbwezo, nambho msiileni Mnungu chindhu chimenecho, pakuti yalembedwa mmalembo ya Mnungu, "Nghani ya kubwezela mbwezo ni njhito yanga, ine sinibwezele Ambuye akamba." 20 Yalembedwa malembo yanjake kuti, "Mdani wako wakakhala ni njala mpache chakudya, wakakhala ni lujho mpache majhi. Pakuti kwa kuchita chimwecho simwachite alenge njhoni kupunda." 21 Siudavomela kulepela ni voipa, nambho ukukhoze kuipa kwa ubwino.