Poolo ni Sila aikidwa mndende
16 Siku limojhi yapo timapita pamalo pampajha pochitila mapembhelo, tidakomana ni mbowa mmojhi wa mkazi uyo wadali ni chiwanda. Mwali mmeneyo wadali ni mzimu woombeza mkati mwake, uwo umampacha nghongono za kuombeza yayo siyachokele mchogolo. Mnamwali mmeneyo wamapacha opata ndalama zambili kwa njhito yake ya kuombeza. 17 Mwali mmeneyo wadamchata Poolo ni ife malo yonjhe yayo timapita, uku niwakweza mvekelo, pokamba, "Wandhu anyiyawa ni atumwi wa Mnungu wa mkulu! Akukambilani umo mukhoza kuomboledwa!" 18 Wadayendekela kukamba chimwecho kwa masiku yambili mbaka mawu yake yadamkwiicha Poolo. Poolo wadang’anamuka ni kuchinyindila chijha chiwanda niwakamba, "Kwa mbhavu za Yesu Kilisito, nikulamula uchoke mkati mwake!" Pampajha chijha chiwanda chidamchoka.