1 Nijhidama, ingakhale siifunika! Chipano sinikambe maloso ni uvunukulo uwo anilangiza Ambuye. 2 Nijhiwa mundhu mmojhi Mkilisito, uyo vyaka khumi ni vinai va pita wadanyakulidwa mbaka ku mwamba kupunda. Sinijhiwa ngati wadali kumeneko kwa thupi kapina kwa mzimu, nambho wajhiwa Mnungu. 3 Nikambanjho, nijhiwa mundhu mmeneyo wadanyakulidwa mbaka kumwamba kwa Mnungu. Nambho sinijhiwa ngati wadali kumeneko kwa thupi kapina kwa mzimu, nambho Mnungu wajhiwa. 4 Kumeneko wadavela vindhu ivo sivifotokozeka ni vindhu ivo sivifunika ata mundhu kuvivela. 5 Sinijhielekele ndande yamundhu ngati mmeneyo, sinijhielekela namwene, nambho ine sinijhielekele unyondi wanga. 6 Nidakafuna kujhielekela sinidakakhala sabobwa, ndande nimakakamba uzene okhaokha. Nambho sinijhichekeleza, dala mundhu waliyonjhe siwadaniona ine wabwino kupunda kulekana ni umo nionekelana kwayayo niyachita ni kukamba. 7 Nambho dala vindhu ivi vavikulu vavunukulidwa visidani chita nijhidamile, nidapachidwa kupweteka mthupi mwanga ngati minga, mthenga wa satana ndeuyo wanibula dala sinidajhielekela kupunda. 8 Nidaapembha kupunda Ambuye mala katatu anichochele chindhu ichi. 9 Nambho wadanikambila, "Ubwino wanga ukukwana pakuti mbhavu zanga zikwanilichidwa ni unyondi." Chimwecho sinijhielekele kwa kukondwela unyondi wanga, dala mbhavu za Kilisito ukhale pa mwamba panga. 10 Chimwecho nivomela unyondi ni kudelela ni kulaga ni mavuto ni machaucho, ndande ya Kilisito, yapo nikhala nyondi, nde yapo nikhala ni mbhavu.
11 Nili ngati asabobwa, anyiimwe nde yao mwanikakamiza kukhala chimwecho. Anyiimwe nde mmafunika kunielekela. Ingakhale ine asati kandhu. Nambho ine asati wamng'ono kusiyana amenewo, "Atumwi waakulu." 12 Yapo nidali kwanu, nidali olimba mtima nikuchita vozizwicha ni vodabwicha ivo vilangiza kuti ine mtumwi. 13 Bwanji, mwachepekeledwa chiyani kusiyana ni magulu ina ya wandhu amkhulupilila Kilisito? Nambho ine sinidafune kukuchauchani kupata mthandizo kwanu? Ngati kuchita chimwecho ni kuipa, nipembha munilekelele! 14 Chipano nilitayali kujha kwanu mala ya katatu. Ndande sinifuna chuma chanu, nambho nikufunani mwachinawene. Wana saikila ndande ya obala wao, nambho obala nde yao aikila ndande ya wana wao. 15 Nili tayali kujhichocha namwene ni kutumila icho nilinacho, ndande ya kukuthangatilani. Ata ngati ioneka kuti umo niendekela kukukondani nde umo chikondi chanu chipunda kuchepekela kwa ine.
16 Nambho simvomele kuti ine sinidali katundu kwanu. Nambho mundhu mwina wakhoza kukamba kuti, "Paulo wadali ochenjela, ni wakunyengani." 17 Bwanji, nidamtuma mthenga waliyonjhe kwanu wajhe kutenga kandhu? 18 Nidampembha ni kumtuma Tito wajhe kwanu, nidamtuma ni mbale wathu mwina. Bwanji, Tito wadatenga kandhu kwanu? Bwanji simujhiwa kuti ife tichogozedwa ni mzimu uujha, ni maendedwe yathu ni yamojhi?
19 Mkhoza kuganiza titojhiteteza tawefe pachogolo panu! Tikamba yameneyo pachogolo pa Mnungu, tili olunjana ni Kilisito. Vindhu vonjhevo ndande ya kukulimbichani anyiimwe okondedwa. 20 Niopa, nikajha kukuphezani asati ngati umo mufunila kuniona, namwe simuniona ngati umo mufunila kuniona. Niopa kukhoza kukhala ni ndeo, njhanje, kufunana, mtafu, kukambana kuipa, kunamizilana, dama ni pwilikiti. 21 Niopa yapo sinijhe ulendo uwo ukujha, Mnungu wanichite ochika kwanu, sinaadandaulile ndande ya ambili yao achita machimo nambho saadalape, akali ni makhumbilo yao yachithupi ni akali kuchita chigololo.