25 Usiku pakati Poolo ni Sila amapembhela ni kumuimbila Mnungu nyimbo za matamando uku omangwidwa wina niwavechela. 26 Kudaveka mvekelo wa chimtingiza mndhaka, icho chidatingiza msingi wa ndende. Pampajha vicheko vidachakuka kwamkamojhi, ni maunyolo yajha adamangidwa omangidwa ameneo yadamasuka ni kugwa panjhi. 27 Yujha mlonda wa ndende yapo wadauka ni kuona vicheko vandende vachekuka, wamaganiza andende athawa, chimwecho wadasolomola upanga wake kuti wajhiphe. 28 Nambho Poolo wadamtana kwa mvekelo waukulu niwakamba, "Usadajhipa pakuti ife taonjhe tili muno!"
29 Yujha mlonda wa ndende wadatanicha nyali, ndiipo wadalowa msanga mkati mwa ndende mujha, wadajhitaya pachogolo pa Poolo ni Sila uku nawatendhemela kwa mandha. 30 Ndiipo wadaatulucha kubwalo ni kukamba, "Olemekezeka nichite chiyani kuti niomboledwe?"
31 Anyiiwo adamuyangha, "Akhulupilile Ambuye Yesu Kilisito, iwe pamojhi ni wandhu amnyumba mwako nde yapo siuomboledwe." 32 Chimwecho Poolo ni Sila adamlalikila uthenga wa Ambuye, yujha mlonda pamojhi ni wandhu wonjhe yao amakhala mnyumba mwake. 33 Ndhawi imweiijha yujha mlonda wa ndende wadaatenga Poolo ni Sila ni kwaachuka mabala yao. Ndiipo yujha mlonda pamojhi ni wandhu wonjhe amnyumba mwake adabatizidwa. 34 Wadaatenga Poolo ni Sila mbaka kukhomo kwake, wadaapacha chakudya. Iye Pamojhi ni wandhu amnyumba mwake adachita pwandho ndande chipano amkhulupilila Mnungu.