Saulo ni Banaba atumidwa
1 Wandhu yawo adamkhulupilila Mnungu ku Antiokia wina adali alosi ni oyaluza, pakati pao padali Banaba, Simioni uyo watanidwa Wakuda, Lukiya uyo wachokela ku mujhi wa Kilene ni Saulo ni Manaeni uyo wadaleledwa pamojhi ni mfumu Helode Antipasi. 2 Yapo amampembha Mnungu ni kumanga kudya, Mzimu Woyela udaakambila, "Nipatulileni Banaba ni Saulo, kuti achite njhito iyo naatanila kuchita."
3 Yapo adamaliza kumanga kudya ni kupembhela, anyiiwo adaasanjika manja Banaba ni Saulo ni kwasiya ajhipita.