44 Achaatate wathu adali ni hema lijha limalangiza kuti Mnungu wali pamenepo. Lidakonjedwa ngati umo Mnungu wadamkambila Musa wachite, kuchokana ni umo wadalangizidwa kuti walikonje. 45 Pambuyo pake, azee wathu wajha adalandilana hema limenelo ayiiwo kwa anyiiwo mbaka Yoshuwa yapo wamachogoza, adalanda jhiko kuchokela kwa maiko yajha yadatopoledwa ni Mnungu pamaso pao. Hemalo lidakhala mjhiko limenelo mbaka pa ndhawi iyo Daudi. 46 Daudi wadakondeledwa ni Mnungu, ni wadapembha Mnungu kuti wamloleze wammangile nyumba umo iye ni Aizilaeli wonjhe akhoza kumlambila. 47 Nambho Solomoni nde uyo wadamanga nyumba ya Mnungu. 48 Ata chimwecho, Mnungu wamkulu wa Kumwamba siwakhala mnyumba yomangidwa ni manja ya mundhu, ngati umo mlosi wakambila,
49 "Ambuye akamba, ‘Kumwamba ni mpando wanga wachifumu,
ni pajhiko lapanjhi ni malo ya kuikapo miyendo yanga.
Nyumba yamtundu wanji iyo simunimangile ine?
Kapina malo yanga yopumulilamo siyakhale yati?
50 Bwanji, vindhu vonjhevi sinidavimange ine kwa manja yanga?’"