17 Helode mwene wake wadalamula Yohana wagwilidwe, waikidwe mndende. Helode wadachita chimwecho ndande ya Helodia uyo wadamkwata, wamkazi mmeneyo wadali wamkazi wa Filipo mphwake wa Helode. 18 Helode wadamchitila chimwecho Yohana ndande wadamkambila, "Osati bwino iwe kumkwata wamkazi wa mphwako!"