Pular para o conteúdo
Publicidade

Marcos 7

Chikhulupililo cha wamkazi mmojhi uyo siwadali Muyahudi

24 Yesu wadachoka pamenepo, nikupita ku mujhi wa Tilo. Kumeneko wadalowa mnyumba imojhi ni siwadafune mundhu wajhiwe, nambho siwadakhoze kujhibisa. 25 Pajha padalipo ni wamkazi mmojhi uyo wadali ni mwali wa chiwanda, yapo wadavela kuti Yesu wali pajha. Wadajha ni kugwada, pachogolo pa myendo ya Yesu. 26 Yapo wadamgwadila wadampembha Yesu wamchoche chiwanda mwali wake, nambho wamkazi mmeneyo wadali osati Muyahudi, uyo wadabadwila ku Foinike mjhiko la Siliya. 27 Yesu wadamkambila, "Asiye wana akhute uti. Pakuti osati bwino kutenga chakudya cha wana ni kwaponyela agalu."

28 Nambho yujha wamkazi wadamyangha, "Ambuye ni chazene icho mwakamba, nambho ata agalu ali panjhi pa meza akudya vakudya ivo vikhalila kwa wana."

29 Yesu wadamkambila wamkazi yujha, "Ndande wayangha bwino, pita kukhomo kwako ni siumpheze mwali wako walama ni chiwanda chamchoka!"

30 Chimwecho wamkazi yujha wadapita kukhomo lake, wadampheza mwana wake wagona pachika, ni chiwanda chathomchoka.

Veja também