14 Yapo wadakamba yameneyo, wadang’anamuka kumbuyo, wadamuona Yesu waima pamenepo, nambho siwadajhiwe kuti nde Yesu. 15 Yesu wadamfunjha, "Maye, ndande yanji mulila? Mumfunafuna yaani?"
Malia wamaganiza osunga busitani, wadamkambila, "Olemekezedwa ngati imwe nde mwaatenga, pepani nipembha munilangize ukomwamuika, sinimtenge."
16 Yesu wadamkambila, "Malia!"
Malia nayo wadang’anamuka, wadamkambila kwa Chihebulania, "Laboni" Mate yake "Oyaluza."