Pular para o conteúdo
Publicidade

Luka 19

Yesu ni Zakayo

1 Yesu wadapita kumujhi wa ku Yeliko, nayo wamapitapita mmikwakwa ya mmujhi umeneo. 2 Padali ni mundhu mmojhi mmujhi mmenemo wamatanidwa Zakayo. Mmeneyo wadali wamkulu wa wandhu wolandila malipilo ni wadali ni chuma chambili. 3 Iye wamafuna wamuone Yesu kuti ni mundhu wamtundu wanji, nambho wadalepela kumuona ndande iye wadali wamfupi, ni wandhu adachuluka. 4 Chimwecho, wadathamangila mchogolo, wadakwela mumtengo wa mkuyu kuti wakhoze kumuona Yesu, pakuti wamajhiwa Yesu wamapita mnjila imeneyo. 5 Yesu yapo wadafika pamalo yameneyo, wadapenya mmwamba mwa mtengo ni kumkambila, "Zakayo, chika chisanga, pakuti lelo sinikhale mlendo kukhomo lako." 6 Zakayo wadachika chisanga ni kumlandila Yesu kwa kukondwela. 7 Wandhu wonjhe yapo adaona yameneyo adayamba kudandaula ni kukamba, "Wapita kukhala mlendo wa mundhu wa machimo."

8 Nambho Zakayo wadaima ni kwaakambila Ambuye, "Vechelani Ambuye! Ine sinaninghe wosauka chuma changa chakumojhi, ningati namlanda mundhu chindhu chalichonjhe, sinimbwezele kanayi."

9 Yesu wadamkambila, "Lelo uomboli wajha mnyumba ino, pakuti uyu nayo ni wa mwana wa mmuna wa Ibulahimu. 10 Pakuti ine mwana wa Mundhu najha kufunafuna ni kulamicha chijha chidataika."

Veja também