25 Nyengo imeneyo kudali mundhu mmojhi mu Yelusalemu uyo wamatanidwa Simiyoni, wadali wovomelezeka ni woopa Mnungu. Iye wamalindilila kujha kwa uomboli wa Izilaeli, ni Mzimu Woyela udali ni iye. 26 Mzimu Woyela udamchimikizila kuti siwafa mbaka yapo siwamuone Kilisito uyo wasanghidwa ni Ambuye. 27 Ndiipo Mzimu wa Mnungu udamchogoza Simiyoni kulowa pa Nyumba ya Mnungu. Anyakubala a Yesu adampeleka mwana wao pa Nyumba ya Mnungu kuti amuchite ngati umo lifunila khalidwe, 28 Simiyoni wadamtenga mwana yujha mmanja mwake uku niwamtamanda Mnungu, pokamba,
29 "Chipano Ambuye mwakwanilicha ahadi zanu,
munilole mbowa wanu nimwalile kwa mtendele.
30 Pakuti nauona uomboli wanu kwa maso yanga,
31 uwo mwaupeleka kuti uonekane kwa wandhu amaiko yonjhe.
32 Dangalila la kwawalila wandhu yawo osati Ayahudi,
ni ukulu kwa wandhu wanu ajhiko la Izilaeli."