Pular para o conteúdo
Publicidade

Luka 7

Yesu wamuhyukicha mwana wa wamkazi uyo wafedwa ni wammuna

11 Yapo wadamaliza yameneyo, Yesu wadapita ku mujhi umojhi uwo utanidwa Nayini, pamojhi ni oyaluzidwa wake ni gulu lalikulu la wandhu yawo wadachogozana nawo. 12 Ndiipo, Yesu yapo wadali pafupi kufika pa chicheko chachikulu cha mujhi, adatulukila wandhu yawo adatenga chitanda cha wammuna mmojhi. Mwana mmweyo wadali wa maye uyo wadafedwa ni wammuna. Ni wandhu ambili a mujhi ujha adali pamojhi ni wamkaziyo. 13 Ambuye Yesu yapo adamuona maye wa mwana yujha, adamlengela lisungu, adakamba, "Osalile." 14 Ndiipo, wadapita ni kuligafya bokosi la chitanda chijha, wandhu yawo adalitenga, adayima. Ndiipo wadanena, "Mnyamata iwe, nikukambila, nyakuka!" 15 Mnyamata wakufa yujha wadanyakuka, ni kukhala, ndiipo wadayamba kunena. Ndiipo Yesu wadampeleka kwa amaye wake. 16 Wandhu wonjhe adali pamenepo adadabwa, nikuyamba kumtamanda Mnungu, naakamba kuti, "Mneneli wamkulu wationekela pakati pathu. Mnungu wafika kwaombola wandhu wake." 17 Nghani zimezi zidaenela ku Yudea pamojhi ni malo yayo yadali pafupi, ni mayiko ina.

Veja também