Pular para o conteúdo
Publicidade

Mateus 15

Chikhulupi cha wamkazi

21 Yesu wadachoka malo yameneyo ni kupita kumijhi ya Tilo ni Sidoni. 22 Wamkazi mmojhi uyo wamakhala mmalo yameneyo, uyo siwadali Myahudi, wadamchata Yesu uku niwalila, niwakamba, "Nilengele lisungu iwe Mwana wa Daudi, mwali wanga wazamwa ni viwanda, wavutika kupunda."

23 Nambho Yesu siwadamuyanghe mau lililonjhe. Chimwecho oyaluzidwa wake adamchata ni kumpembha kupunda, "Mkambile wachoke ndandeyake watichata uku niwatibulila phokoso."

24 Yesu wadaayangha, "Ine natumidwa kwa wandhu ajhiko la Izilaeli yawo ali ngati mbelelepe izo zataika."

25 Wamkazi yujha wadajha ni kumgwadila Yesu, niwapembha, "Pepani Ambuye mnithangatile."

26 Yesu wadayangha, "Osati bwino kutenga chakudya cha wana ni kwaaponyela agalu."

27 Wamkazi yujha wadayangha, "Yetu Ambuye, nambho ata agalu akudya vakudya ivo vikugwa panjhi mbuye wake yapo wakudya."

28 Ndiipo Yesu wadamuyangha, "Wamkazi iwe, chikhulupi chako chachikulu, siuchitilidwe icho udachipembha." Pampajha mwali wake wadalama.

Veja também