Publicidade

Mateus 2

Alendo kuchokela ku dela la kumwela

1 Yesu wadabadwa ku mujhi wa Beselehemu mjhiko la Yudea. Ndhawi imeneyo Helode wadali mfumu. Yesu yapo wadandobadwa wandhu yawo amajhiwa icho sichichokele adafika ku Yelusalemu 2 adaafunjha, "Walikuti mwana uyo wabadwa Mfumu wa Ayahudi? Pakuti tayiona ndhondwa yake kudela la kumwela ni nafenjho tajha kumulambila."

3 Mfumu Helode ni wandhu wonjhe yawo adali ku Yelusalemu yapo adavela nghani zimenezo wadavutika mumtima. 4 Mfumu Helode wadaatana pamojhi waakulu ajhukulu ni woyaluza mathauko wadaafunjha, "Kilisito wabadwila kuti?"

5 Adamuyangha, "Wabadwila mmujhi wa Beselehemu mjhiko la Yudea pakuti nde umo wadalembela mlosi,

6 ‘Iwe Beselehemu mujhi wa Yudea,

mujhi wanu ni waukulu pakati pa mijhi yojhiwika mu Yudea.

Pakuti kwanu siwachokele mchogoleli,

uyo siwaachogoze wandhu wanga Izilaeli.’ "

7 Helode wadaatana kwa chisisi wandhu wajha ajhiwa yayo siyachokele kwa kupenya ndhondwa ni kwaafunjha ndhawi iyo idaonekana ndhondwa. 8 Wadaatuma ku Beselehemu ni kwaakambila, "Mapitani mkafunjhile bwino nghani za mwanayo. Yapo simumuone mbwele munikambile kuti nanenjho nipite nikamulambile."

9 Yapo adamaliza kumvechela mfumu adachoka ni ndhondwa iyo adaiwona kuchoka kudela la kumwela idaachogoza ni kuima pajha wadali mwana. 10 Yapo adaiona ndhondwa ijha adakondwa kupunda. 11 Ndiipo adalowa mnyumba ni adamuona mwana pamojhi ni Maliya maye wake. Adagwada ni kumlambila. Adamasula mbhaso zao ni kumpacha mwana zaabu ni ubani ni mnghwala uwo utanidwa manemane.

12 Ndiipo Mnungu adaonya kumaloto kuti asadabwelela kwa Helode. Chimwecho adabwela kujhiko lawo kwa kupitila njila yina.

Kuthawila ku Misili

13 Wandhu yapo adatochoka mtumiki wa Ambuye wadamujhela Yusufu kumaloto ni kumkambila kuti, "Nyamuka umutenge mwana ni maye wake mthawile Kumisili. Mkakhale kumweko mbaka yapo sinikukambile pakuti Helode wafuna kuti wamphe mwanayo."

14 Chimwecho Yusufu wadauka wadamtenga mwana ni maye wake usiku umweujha. Adapita kujhiko la Misili. 15 Adakhala kumweko mbaka yapo wadamwalila Helode. Chindhu chimenecho chidachitika dala yakwanile mau yayo yadalembedwa ni Ambuye kupitila mlosi kunena kuti, "Nidamtana mwana wanga kuchokela kujhiko la Misili."

Wana waang'onoang'ono aphedwa

16 Helode yapo wadajhiwa kuti wanyengedwa ni wojhiwa yayo siyachokele kwa kupenya ndhondwa wadakwiya kupunda. Wadalamula wana wonjhe waachimuna yawo adali mu Beselemu ni mijhi iyo idali pafupi ni Beselemu aphedwe. Kuyambila wana yawo adali ni vyaka viwili ni kuchika panjhi. Kuyambila siku lijha wandhu wajha yapo adaiona ndhondwa.

17 Ndiipo chijha chidakambidwa kwa njila ya mlosi Yelemiya chidakwanila,

18 "Chililo chaveka Kulama

chililo ni kubuula kwa kukulu,

Laheli walilila wana wake,

Siwafuna kupembezedwa

pakuti wonjhe amwalila."

Kubwela kuchokela ku Misili

19 Pambuyo pa Helode kumwalila mtumiki wa Ambuye wadamuonekela Yusufu ku maloto kujhiko la Misili. 20 Wadaakambila kuti, "Nyakuka umtenge mwana ni maye wake ubwelele kujhiko la Izilaeli pakuti wandhu yawo amafuna kumpha mwana athomwalila." 21 Chimwecho Yusufu wadanyakuka. Wadamtenga mwana ni maye wake ni kupitanayo kujhiko la Izilaeli.

22 Nambho Yusufu yapo wadavela kuti Alikelao mwana wa Helode uyo wadali Mfumu wa kujhiko la Yudea wadaalisi atate wake wadaopa kupita kumeneko. Wadapita kumujhi wa Galilaya ndande wadaonyedwa mmaloto. 23 Nayo wadapita kukhala kumujhi utanidwa Nazaleti kuti yakwanile mawu yayo yadanenedwa ni mlosi, "Siwatanidwe Mnazaleti."

Veja também

Publicidade
Bíblia Online Bíblia Online

Bíblia Online • Versão: 2026-06-15_21-32-39-