Pular para o conteúdo
Publicidade

Lucas 16

Mundhu wopata ni Lazalo

19 "Padali mundhu mmojhi wopata uyo wamavala njhalu zokhadwa zamtengo wapamwamba, uyo wamakhala kwa anasa masiku yonjhe. 20 Pachicheko chake padali wosauka mmojhi, jina lake Lazalo, uyo wadajhala vilonda thupi lambhumbhu. 21 Lazalo wamakhumbila kudya vakudya vokhalila ivo vimagwa panjhi pa meza ya mundhu wopatayo. Ata agalu amajha kumnyambita vilonda vake. 22 Pambuyo wosauka Lazalo wadamwalila, atamuki akumwamba Amnungu adamtenga ni kumuika wakhale pamojhi ni Ibulahimu. Mundhu wopata yujha nayonjho wadamwalila ni wadaikidwa mmanda. 23 Mundhu wopata yapo wadali mmavuto yayakulu kugahena, wadapenya, wadamuona Ibulahimu kwapatali, ni pafupi pake wadalipo Lazalo. 24 Chimwecho, mundhu wopatayo wadamtana Ibulahimu, Atate Ibulahimu, nilengeleni lisungu, mumtume Lazalo wabize chala chake mmajhi kuti wajhe kuzizilicha lilime langa, chifuko nipata mavuto kupunda kuno ku Gahena.25 Nambho Ibulahimu wadamuyangha, Mwana wanga, kumbukila yapo udali wamoyo pajhiko udathopata vindhu vabwino ivo udavikhumbila, ni Lazalo wadapata mavuto. Nambho chipano, Lazalo wathilidwa mtima, ni iwe uvutika. 26 Ata chimwecho, pakati panu ni ife pali jhenje lalikulu, kuti yawo afuna kuchoka kuno kujha kumeneko sadakhoza, kapina yawo afuna kuchoka kumeneko kujha kuno kwathu alepele.27 Ndiipo wopatayo wadampembha kupunda, Basi nikupembhani atate wanga a Ibulahimu, mumtume Lazalo wapite kukhomo kwa achabale wanga. 28 Nili ni achabale asano kumeneko, wapite wakaonye kuti naonjho sadafika kumalo yano ya mavuto.29 Nambho Ibulahimu wadamuyangha, Achabale wako ali ni mathauko ya Musa ni malembo ya alosi, asiye ayavechele yameneyo.30 Nambho wopatayo wadakambanjho, Atate wanga a Ibulahimu, ngati mundhu wakachoka kuno nikwapitila, salape machimo yawo.31 Ndiipo Ibulahimu wadamuyangha, Ngati sayavela mathauko ya Musa pamojhi ni malembo ya alosi, sangakhoze kuvela ata ngati wakapitila mmojhi uyo wahyuka kuchokela kwa akufa."

Veja também