Pular para o conteúdo
Publicidade

Lucas 18

Chifani cha wamkazi wafedwa ni mmunake ni mlamuli wa milandu

1 Ndiipo Yesu wadaakambila ochatila chifani ichi kwaalangiza umo afunikila kupembhela popande kulema. 2 Wadakamba, "Mmujhi umojhi padali mlamuli wa milandu mmojhi uyo siwamamuope Mnungu kapina kusamala mundhu. 3 Mmujhi umeneo padali maye mmojhi uyo wadafedwa ni mmunake, uyo wamajha kwaiye kila mala kumpembha kupunda, Chonde munithangatile kuti nipate chuma changa kuchoka kwa mdani wanga.4 Pasiku zambili mlamuli wa milandu yujha siwamafune kumthangatila maye yujha wafedwa ni mmunake. Nambho pothela wadajhikambila mumtima, Ingakhale kuti ine sinimuopa Mnungu kapina kusamala mundhu, 5 nambho pakuti uyu wamkazi wafedwa ni mmunake wanichaucha kupunda, sinimthangatile, nikasiya kumthangatila siwayendekele kunichaucha kwakujha kwanga tetete!"

6 Ndiipo, Ambuye adakamba, "Muyaganizile kupunda yayo wadayakamba mlamuli wa milandu uyo siwachita njhito yake umo ifunikila. 7 Bwanji, Mnungu siwaathangatila wandhu wasangha yawo ampembha kupunda popande kulema usana ni usiku? Bwanji, siwachedwa kwaapacha? 8 Nikukambilani, kuti siwakupacheni yayo mfuna kwa chisanga. Bwanji, yapo siwafike ine mwana wa mundhu, bwanji sinapheze wandhu ali ni chikkulupi pano pajhiko?"

Veja também