Yesu wapelekedwa Kunyumba ya Mnungu
22 Masiku yosamba naye mwana yapo yadakwana, ngati umo lidali thauko la Mnungu ilo wadampacha Musa, anyakubala wake adamtenga mwana ni kupitanayo ku Yelusalemu kuti akampeleke pamaso pa Ambuye. 23 Ngati umo idalembedwela mu thauko la Ambuye kuti, "Kila mwana wammuna wachisamba siwapatulidwe ndande ya Ambuye." 24 Naonjho adapita kuti akachoche mahoka kwa Mnungu, maliunda yawili ya nghunda ngati lifunikila thauko la Ambuye.
25 Nyengo imeneyo kudali mundhu mmojhi mu Yelusalemu uyo wamatanidwa Simiyoni, wadali wovomelezeka ni woopa Mnungu. Iye wamalindilila kujha kwa uomboli wa Izilaeli, ni Mzimu Woyela udali ni iye. 26 Mzimu Woyela udamchimikizila kuti siwafa mbaka yapo siwamuone Kilisito uyo wasanghidwa ni Ambuye. 27 Ndiipo Mzimu wa Mnungu udamchogoza Simiyoni kulowa pa Nyumba ya Mnungu. Anyakubala a Yesu adampeleka mwana wao pa Nyumba ya Mnungu kuti amuchite ngati umo lifunila khalidwe, 28 Simiyoni wadamtenga mwana yujha mmanja mwake uku niwamtamanda Mnungu, pokamba,
29 "Chipano Ambuye mwakwanilicha ahadi zanu,
munilole mbowa wanu nimwalile kwa mtendele.
30 Pakuti nauona uomboli wanu kwa maso yanga,
31 uwo mwaupeleka kuti uonekane kwa wandhu amaiko yonjhe.
32 Dangalila la kwawalila wandhu yawo osati Ayahudi,
ni ukulu kwa wandhu wanu ajhiko la Izilaeli."
33 Atate wake ni amake a Yesu amangozizwa mawu yonjhe yayo yamakambidwa yakuusu mwana. 34 Simiyoni wadaapacha mwawi, ni kumkambila Maliya make wa mwana, "Mwana uyu siwakhale chifuko cha khugwa ni kuomboka wandhu ambili mu Izilaeli. Iye siwakhale chizindikilo chochokela kwa Mnungu icho sichikanidwe ni wandhu ambili, 35 ni maganizo ya wandhu ambili siyaonekane padanga, ni iwe umwene wake siudandaule kupunda."
36 Kudali wamkazi mmojhi mlosi wamatanidwa Ana, mwana wamkazi wa Fanueli, wafuko la Asheli wadali mzee kupunda. Pa umwali wake wadakwatiwa ni kukhala ni mmunake kwa vyaka saba, ndiipo mmunake wadamwalila. 37 Chimwecho, wadakhala wafedwa ni mmunake mbaka yapo wadali ni vyaka semanini ni vinayi. Ndhawi yonjheyi wamakhala pa Nyumba ya Mnungu nambho wamamlambila Mnungu usiku ni usana popande kudya ni wapembhela. 38 Ndhawi imweyo Ana wadatulukila pachogolo pa Yusufu ni Maliya, wadamuyamika Mnungu, ni kukamba nghani za mwanayo kwa wandhu wonjhe yawo amalindilila uomboli wa ku Yelusalemu.