Asadukayo amfunjha Yesu nghani za kuhyuka
23 Siku limwelo akumojhi wa Asadukayo, yawo akamba, palibe kuhyuka kwa wandhu, adampitila Yesu, adamkambila, 24 "Oyaluza, Musa wadakamba ngati mundhu wammuna wamwalila popande kusiya mwana, mbale wake wamkwate wamkazi wafedwa ni mmunake kuti wambalile mbalewake wana. 25 Pano pathu padali ni abale saba. Oyamba wadakwata ni kumwalila, ndande wadalibe mwana, mpwake wadalowa chokolo wamkazi mmeneyo. 26 Chindhu chimchijha chidamchitikila mbale wa kawili ni waka tatu mbaka wa saba. 27 Pothela wamkazi mmeneyo nayo wadamwalila. 28 Akahyuka wamkazi siwakhale wayani pakuti wonjhe saba adamkwata."
29 Yesu wadayangha wajha Asadukayo, "Mwasokelela anyiimwe, pakuti simujhiwa malembo yoyela kapina mbhavu za Mnungu. 30 Wandhu yapo ahyuka palibe kukwata kapena kukwatiwa, siakhale ngati mtumiki wa kumwamba. 31 Pa nghani za kuhyuka, simdajhiwe chijha wadakukambilani Mnungu? Wadaakambila, 32 ‘Ine nde Mnungu wa Ibulahimu ni Mnungu wa Isaka ni Mnungu wa Yakobo.’ Chimwecho, Mnungu osati Mnungu wa wandhu omwalila, nambho ni Mnungu wa wandhu amoyo."
33 Gulu la wandhu yapo lidavela mawu yameneyo lidazizwa mayaluzo yake.