13 Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu?
Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake,
"Iye sandiyimba mlandu?"
14 Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,
mumaganizira zochitapo kanthu.
Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti
Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.