6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima;
pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Pumula iwe moyo wanga,
pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,
maso anga ku misozi,
mapazi anga kuti angapunthwe,
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova
mʼdziko la anthu amoyo.