Pular para o conteúdo
Publicidade

Salmos 119

9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?

Akawasamala potsata mawu anu.

10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;

musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.

11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga

kuti ndisakuchimwireni.

12 Mutamandike Inu Yehova;

phunzitseni malamulo anu.

13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse

amene amachokera pakamwa panu.

14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu

monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.

15 Ndimalingalira malangizo anu

ndipo ndimaganizira njira zanu.

16 Ndimakondwera ndi malamulo anu;

sindidzayiwala konse mawu anu.

Gimeli

Veja também