7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu?
Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko;
ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko.
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa,
ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera,
dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.