Pular para o conteúdo
Publicidade

MASALIMO 139

7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu?

Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?

8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko;

ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko.

9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa,

ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,

10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera,

dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.

Veja também