Salimo la Davide.
1 Atamandike Yehova Thanthwe langa,
amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;
zala zanga kumenya nkhondo.
2 Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,
linga langa ndi mpulumutsi wanga,
chishango changa mmene ine ndimathawiramo,
amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.