Pular para o conteúdo
Publicidade

Salmos 30

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.

1 Ndidzakukwezani Yehova,

chifukwa mwanditulutsa kwakuya,

ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.

2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo

ndipo Inu munandichiritsa.

3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,

munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.

4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;

tamandani dzina lake loyera.

5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi

koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;

utha kuchezera kulira usiku wonse,

koma chimwemwe chimabwera mmawa.

6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,

"Sindidzagwedezekanso."

7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,

munachititsa phiri langa kuyima chilili;

koma pamene munabisa nkhope yanu,

ndinataya mtima.

8 Kwa Inu Yehova ndinayitana;

kwa Ambuye ndinapempha chifundo;

9 "Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga

ngati nditsikira ku dzenje?

Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?

Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?

10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;

Yehova mukhale thandizo langa."

11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;

munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,

12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

Veja também