Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1 Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;
musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;
mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Tcherani khutu lanu kwa ine,
bwerani msanga kudzandilanditsa;
mukhale thanthwe langa lothawirapo,
linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,
chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Ndimasuleni mu msampha umene anditchera
pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;
womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.