Pular para o conteúdo
Publicidade

Salmos 32

1 Ngodala munthu

amene zolakwa zake zakhululukidwa;

amene machimo ake aphimbidwa.

2 Ngodala munthu

amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye

ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.

3 Pamene ndinali chete,

mafupa anga anakalamba

chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.

4 Pakuti usana ndi usiku

dzanja lanu linandipsinja;

mphamvu zanga zinatha

monga nthawi yotentha yachilimwe.

Sela

5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu,

sindinabise mphulupulu zanga.

Ndinati, "Ine ndidzawulula

zolakwa zanga kwa Yehova,

ndipo Inu munandikhululukira

mlandu wa machimo anga."

Sela

6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo

pomwe mukupezeka;

ndithu pamene madzi amphamvu auka,

sadzamupeza.

Veja também