7 Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali!
Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu
amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu;
Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
9 Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo;
mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.