4 "Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga
ndi chiwerengero cha masiku anga;
mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,
kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;
moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.
Sela
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:
Iye amangovutika koma popanda phindu;
amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.