1 Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Imbani ulemerero wa dzina lake;
kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Nenani kwa Mulungu, "Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu!
Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri
kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu;
limayimba matamando kwa Inu;
limayimba matamando pa dzina lanu."
Sela.