Ndakatulo ya Asafu.
1 Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa;
mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo,
ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa,
zimene makolo athu anatiwuza.
4 Sitidzabisira ana awo,
tidzafotokozera mʼbado wotsatira
ntchito zotamandika za Yehova,
mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.